Mawu Amunsi
d Mau a Mulungu alinso ndi mfundo zimene zingaoneke “zovuta kuzimvetsa,” kuphatikizapo mbali zina zimene Paulo analemba. Komabe, onse amene analemba Baibulo anatsogoleledwa ndi mzimu woyela. Masiku ano, mzimu wa Mulungu umathandizanso Akristu oona kumvetsetsa Baibulo, “ngakhale zinthu zozama za Mulungu.”—2 Pet. 3:16, 17; 1 Akor. 2:10.