Mawu Amunsi
a Ena mwa anthu amenewa ndi Tacitus, amene anabadwa mu 55 C.E. Iye analemba kuti Akristu anatengela dzinali kwa “Kristu” amene Pontiyo Pilato, mmodzi mwa olamulila athu, anamulamula kuti azunzidwe ndi kuphedwa mu ulamulilo wa mfumu Tiberiyo.” Enanso amene analemba za Yesu anali Suetonius, (wa m’nthawi ya atumwi), wolemba mbili yakale waciyuda Josephus (wa m’nthawi ya atumwi), ndi Pliny Wamng’ono amene anali bwanamkubwa wa ku Bituniya (wa kumayambililo kwa zaka za m’ma 100 C.E).