Mawu Amunsi
a Yosefe amachulidwa kotsiliza m’Malemba pamene Yesu anali na zaka 12. Pamene Yesu anacita cozizwitsa cake coyamba, cimene ndi kusandutsa madzi kukhala vinyo, Yosefe sachulidwako. Iye sachulidwakonso ngakhale pa zocitika zina za pambuyo pake. Panthawi imene Yesu anali pamtengo wozunzikilapo, anapatsa mtumwi Yohane udindo wosamalila Mariya. Yosefe akanakhala kuti anali moyo, Yesu sakanacita zimenezi.—Yoh. 19:26, 27.