Mawu Amunsi
a Mkhristu angasankhe kukhala na mfuti n’colinga cakuti aziphela nyama kuti azidya kapena kuti adziteteze ku nyama zolusa. Koma panthawi imene sakuiseŵenzetsa, ayenela kucotsamo mpholopolo, kapenanso kuimasula, ndi kuisungila pa malo otetezeka. Kumene malamulo salola munthu kukhala na mfuti, kapena kumene kuli malamulo a kasewenzetsedwe ka mfuti, Akhristu ayenela kutsatila malamulowo.—Aroma 13:1.