Mawu Amunsi
a Timoteyo anali mlaliki waluso wa uthenga wabwino. Ngakhale n’conco, mtumwi Paulo anamulimbikitsa kupitabe patsogolo kuuzimu. Cifukwa cotsatila malangizo a Paulo amenewo, iye anacita zambili potumikila Yehova, ndiponso anakhala wothandiza kwambili kwa abale na alongo ake. Mofanana na Timoteyo, kodi mumafunitsitsa kucita zambili potumikila Yehova komanso okhulupilila anzanu? Sitikaikila. Ni zolinga ziti zimene zingakuthandizeni kucita zimenezo? Nanga mungacite ciyani kuti mudziikile zolingazo na kuzikwanilitsa?