Mawu Amunsi
a Yehova anatipatsa mphatso yabwino kwambili—mphatso ya kulankhula. Koma n’zacisoni kuti anthu ambili saiseŵenzetsa bwino mphatsoyi mmene iye afunila. N’ciyani cingatithandize kuti mawu athu azikhala abwino, komanso olimbikitsa m’dzikoli limene makhalidwe akungoipilaipila? Kodi tingam’kondweletse bwanji Yehova mwa mawu athu tikakhala mu ulaliki, pa misonkhano ya mpingo, komanso poceza na ena? Nkhani ino iyankha mafunso amenewa.