Mawu Amunsi
a Kucita mantha n’cibadwa, ndipo kungatiteteze ku zinthu zoopsa. Koma kukhala na mantha osayenela si kwabwino cifukwa kungatigwetsele m’mavuto. Motani? Satana angagwilitsile nchito mantha amenewo kuti atipangitse kupanga cisankho colakwika. Conco, tiyenela kuyesetsa kugonjetsa mantha otelowo. Kodi n’ciyani cingatithandize? Monga tionele m’nkhani ino, tikakhulupilila kuti Yehova ali ku mbali yathu komanso kuti amatikonda, tidzakwanitsa kugonjetsa mantha alionse.