Mawu Amunsi
a Padziko lonse lapansi, mamiliyoni a anthu ophatikizapo amuna, akazi, ndiponso ana akulalikila uthenga wabwino mokangalika. Kodi ndinu mmodzi wa iwo? Ngati n’telo, ndiye kuti mukugwila nchito pansi pa uyang’anilo wa Ambuye wathu, Yesu Khristu. M’nkhani ino, tikambilane umboni woonetsa kuti Yesu ndiye akutsogolela nchito yolalikila masiku ano. Tikamaiganizila mfundo imeneyi, tidzakhala ofunitsitsa kum’tumikilabe Yehova motsogoleledwa na Khristu.