Mawu Amunsi
b KUFOTOKOZELA MAWU ENA: “Paradaiso wauzimu” ni mkhalidwe wacitetezo cauzimu umene tilimo mmene tikulambila Yehova mogwilizana. M’paradaiso wauzimu ameneyu tili na cakudya cauzimu camwana alilenji cosaipitsidwa na mabodza a zipembedzo zonyenga. Cina, timagwilanso nchito yokhutilitsa yolalikila uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu. Tili pa ubale wolimba na Yehova, ndiponso timakhala mwamtendele na abale komanso alongo athu acikondi amene amatithandiza kupilila mwacimwemwe zovuta za paumoyo. Timaloŵa m’paradaiso wauzimu ameneyu tikayamba kulambila Yehova m’njila yoyenela, komanso pamene ticita zonse zotheka kuti titengele citsanzo cake.