Mawu Amunsi
a Kuti tipilile mokhulupilika m’masiku ano otsiliza, tiyenela kupitiliza kukhulupilila Yehova na gulu lake. Mdyerekezi amagwilitsa nchito mayeso kuti atipangitse kuleka kukhulupilila Mulungu. M’nkhani ino, tikambilane zinthu zitatu zimene Mdyerekezi amagwilitsa nchito potiyesa, komanso zimene tingacite kuti tikhalebe okhulupilika kwa Yehova na gulu lake.