Mawu Amunsi
a Yehova analonjeza kuti anthu amene amam’konda adzawapatsa mtendele. Kodi mtendele umene Mulungu amatipatsa n’ciyani? Nanga tingaupeze bwanji? Kodi kukhala na “mtendele wa Mulungu” kungatithandize bwanji pakabuka matenda, pakacitika matsoka azacilengedwe, kapena tikamazunzidwa? Nkhani ino iyankha mafunso menewa.