Mawu Amunsi
a Pamene tili mkati mwa mayeso, tingaone monga kuti Yehova sakutithandiza. Koma mayesowo akatha m’pamene timaona kuti Yehova anatithandiza. Komabe, zocitika pa umoyo wa Yosefe zitiphunzitsa mfundo yofunika kwambili yakuti, Yehova angatithandize kupambana ngakhale pamene tili pa mayeso. Nkhani ino ifotokoze mmene amacitila zimenezi.