Mawu Amunsi
a Tonsefe alambili a Yehova timayesetsa kuŵelenga Mawu ake tsiku lililonse. Anthu enanso ambili amaiŵelenga Baibo, koma zimene amaŵelengazo sazimvetsetsa. Ni mmenenso zinalili kwa anthu ena m’nthawi ya Yesu. M’nkhani ino, tikambilane zimene Yesu anauza anthu amene amaŵelenga Mawu a Mulungu, na zimene tiphunzilapo kuti tizipindula kwambili poŵelenga Baibo.