Mawu Amunsi
a Kuti tipite patsogolo na kukayenelela ubatizo, coyamba, tikhale na colinga cabwino. Cotsatila, titenge masitepe ofunikila. Pogwilitsa nchito citsanzo ca nduna ya ku Itiyopiya, tikambilane masitepe amene wophunzila Baibo angatenge kuti akayenelele ubatizo.