Mawu Amunsi
a Cilengedwe ca Yehova ni cocititsa cidwi kwambili. Kungoyambila pa zinthu zamphamvu monga dzuŵa mpaka ku zinthu zofewa monga maluŵa, nchito zake zonse timacita nazo cidwi. Cilengedwe cimatiphunzitsanso makhalidwe a Yehova. M’nkhani ino, tikambilane cifukwa cake tiyenela kupatula nthawi yoyang’ana zacilengedwe mwacidwi, komanso mmene kucita zimenezi kungatithandizile kumuyandikila Mulungu wathu.