Mawu Amunsi
a Abale na alongo ambili amakumbukila nthawi yosangalatsa imene anali kuyang’ana cilengedwe na makolo awo. Iwo sanaiŵale mmene makolo awo anaseŵenzetsela nthawiyo powaphunzitsa za makhalidwe a Yehova. Ngati muli na ana, kodi mungasewenzetse bwanji cilengedwe powaphunzitsa za makhalidwe a Mulungu? Nkhani ino iyankha funso limeneli.