Mawu Amunsi
c Mabuku a Uthenga Wabwino, amafotokoza zocitika zokhudza zozizwitsa za Yesu zoposa 30. Kuwonjezela apo, nthawi zina zozizwitsa zingapo zimaphatikizidwa m’cocitika cimodzi. Mwacitsanzo, panthawi ina “anthu onse a mumzinda” wina wake anapita kwa iye ndipo “anacilitsa ambili amene anali kudwala.”—Maliko 1:32-34.