Mawu Amunsi
a Ngati munthu amene mumam’konda anamwalila, mosakayikila lonjezo lakuti akufa adzauka limakutonthozani kwambili. Koma kodi mungawafotokozele motani ena cifukwa cake mumakhulupilila lonjezolo? Nanga mungalimbitse bwanji cikhulupililo canu pa ciyembekezo cakuti akufa adzauka? Colinga ca nkhani ino ni kuthandiza tonsefe kulimbitsa cikhulupililo cathu pa ciyembekezo ca kuuka kwa akufa.