Mawu Amunsi
a Tikamapeleka ndemanga pa misonkhano ya mpingo, timalimbikitsana wina na mnzake. Ngakhale n’telo, ena amadodoma kupelekapo ndemanga. Koma ena amasangalala kupelekapo ndemanga, ndipo amafuna kuti azipatsidwa mwayi woyankhapo woculukilapo. Pa mbali ziŵilizi, kodi tingaonetse bwanji kuti timaganizila ena, kotelo kuti tonse tilimbikitsidwe? Nanga tingacite ciyani kuti ndemanga zathu zizilimbikitsa abale na alongo pa cikondi na nchito zabwino? Tikambilane zimenezi m’nkhani ino.