Mawu Amunsi
a Mu 1 Atesalonika caputala 5 muli mafanizo angapo otiphunzitsa za tsiku la Yehova la kutsogolo. Kodi “tsiku” limenelo n’ciyani? Nanga lidzafika motani? Ndani adzapulumuke pa tsikulo? Nanga ndani amene sadzapulumuka? Kodi tingalikonzekele bwanji? Tipeza mayankho pa mafunsowa pokambilana mawu a mtumwi Paulo.