Mawu Amunsi
a Cisautso cacikulu cidzayamba posacedwa. Makhalidwe monga kupilila, cifundo, na cikondi, adzatithandiza kukonzekela nthawi yovuta kwambili imeneyo m’mbili yonse ya anthu. Tiona mmene Akhristu oyambilila anakulitsila makhalidwe amenewa, mmene tingatengele citsanzo cawo, komanso mmene makhalidwewa angatithandizile kukonzekela cisautso cacikulu.