Mawu Amunsi
a Kungocokela m’nthawi ya Adamu na Hava, Satana wakhala akulimbikitsa mfundo yakuti anthu ayenela kusankha okha cabwino kapena coipa. Amafuna kuti tiziyendela mfundo imeneyi ponena za malamulo a Yehova, komanso malangizo a gulu amene timalandila. Nkhani ino itithandiza kupewa mzimu wofala umenewu wa dziko la Satanali. Itithandizanso kukhala otsimikiza mtima kuimabe zolimba ku mbali ya Yehova.