Mawu Amunsi
a Atumiki a Yehova acinyamata amakumana na zocitika zimene zimayesa kulimba mtima kwawo, na kukhulupilika kwawo kwa Yehova. Anzawo a m’kalasi angamawanyodole pokhulupilila kuti zinthu zinacita kulengedwa. Kapena acinyamata anzawo angamawaseke cifukwa cotumikila Mulungu, na kutsatila malamulo ake. Koma monga tionele m’nkhani ino, aja amene amatengela citsanzo ca mneneli Danieli, komanso amene amatumikila Yehova molimba mtima ndiponso mokhulupilika, amakhaladi anzelu.