Mawu Amunsi
a Baibo imaonetsanso kuti Yehova amacita zinthu “cifukwa ca dzina lake.” Mwacitsanzo, iye amatsogolela anthu ake, kuwathandiza, kuwapulumutsa, kuwakhululukila, komanso kuwasunga na moyo. Amacita zonsezi cifukwa ca dzina lake lalikulu, lakuti Yehova.—Sal. 23:3; 31:3; 79:9; 106:8; 143:11.