Mawu Amunsi
f MAWU OFOTOKOZELA ZITHUNZI: Alongo aŵili akupemphela asanadzaze fomu yofunsila Sukulu ya Alengezi a Ufumu. Patapita nthawi, wina akuitanidwa pamene wina sanaitanidwe. M’malo mokhumudwa, mlongo amene sanaitanidwe akupemphela kwa Yehova kuti am’thandize kuzindikila njila zina zimene angawonjezele utumiki wake. Ndiyeno, akulemba kalata ku ofesi ya nthambi yofunsila kukatumikila ku malo osoŵa.