Mawu Amunsi
c Kuseŵeletsa malisece a munthu wina ni m’citidwe wa za ciwelewele umene ungafunike kusamalidwa na komiti ya ciweluzo. Kuseŵeletsa maŵele komanso kukambitsilana za ciwelewele pa meseji kapena pa foni, ni makhalidwe odetsa. Ndipo angafune cisamalilo ca komiti ya ciweluzo malinga na mmene zinthuzo zinacitikila.