Mawu Amunsi
d MAWU OFOTOKOZELA CITHUNZI: Mtsikana amene analeka kutumikila Yehova wakumbukila zimene anaphunzila za kugwa kwa “Babulo Wamkulu.” Cotelo akuyambilanso kutumikila Yehova ndipo akubwelelanso kwa makolo ake a Cikhristu. Ngati zotelezi zingadzacitike, tiyenela kutengela Atate wathu wa kumwamba amene ni wacifundo komanso wacikondi, na kusangalala kuti wocimwa wabwelela kwa iye.