Mawu Amunsi
d Mfumu Asa anacita macimo aakulu. (2 Mbiri 16:7, 10) Ngakhale n’telo, Baibo imakamba kuti iye anacita zoyenela m’maso mwa Yehova. Ngakhale kuti poyamba iye anakana uphungu, n’kutheka kuti pambuyo pake analapa. Yehova anaona zabwino zambili zimene iye anacita kuposa zoipa. Ndipo cofunika kwambili n’cakuti iye analambila Yehova yekhayo, ndipo anayesetsa mwamphamvu kuthetsa kulambila mafano mu ufumu wake.—1 Maf. 15:11-13; 2 Mbiri 14:2-5.