Mawu Amunsi
a KUFOTOKOZELA MAWU ENA: M’Baibo, mawu akuti “ucimo” angatanthauze zinthu zoipa zimene munthu angacite, zomwe n’zosagwilizana na miyeso ya Yehova ya makhalidwe abwino. Koma nthawi zina mawu akuti “ucimo” angatanthauze kupanda ungwilo kumene tinatengela kwa Adamu. Ndipo tonsefe timafa cifukwa ca ucimo umenewu umene tinatengela kwa Adamu.