Mawu Amunsi
f Baibulo silikamba mwachuchuchu zoyenela kapena zosayenela kucita pa nkhani yakucipinda pakati pa mwamuna ndi mkazi wake. Mwamuna aliyense wokwatila wacikhristu pamodzi ndi mkazi wake, ayenela kupanga zisankho pa nkhani imeneyi zoonetsa kuti amalemekeza Yehova, amafuna kusangalatsana bwino, komanso zimene zidzawasiya ndi cikumbumtima coyela. Koma iwo sayenela kukambilana cisawawa ndi anthu ena mmene amaonetselana cikondi mu ukwati wawo.