LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 2 Akorinto 3
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 2 Akorinto

      • Makalata ocitila umboni (1-3)

      • Atumiki a cipangano catsopano (4-6)

      • Ulemelelo wopambana wa cipangano catsopano (7-18)

2 Akorinto 3:3

Mawu amunsi

  • *

    Kucokela ku Cigiriki, “pa zolembapo za mnofu, m’mitima.”

2 Akorinto 3:16

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    4/2018, tsa. 9

2 Akorinto 3:17

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    11/2018, masa. 19-20

    4/2018, masa. 8-9

2 Akorinto 3:18

Mawu amunsi

  • *

    Kucokela ku Cigiriki, “kucoka pa ulemelelo, kupita pa ulemelelo wina.”

  • *

    Ma Baibo ena amati, “mwa mzimu wa Yehova.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
2 Akorinto 3:1-18

Kalata Yaciwiri kwa Akorinto

3 Kodi tayambanso kudzicitila tokha umboni? Kapena tikufunikila makalata oticitila umboni obwela kwa inu kapena ocokela kwa inu mofanana ndi anthu ena? 2 Inuyo ndinu kalata yathu, yolembedwa pamitima yathu, yodziwika komanso yowelengedwa ndi anthu onse. 3 Pakuti n’zoonekelatu kuti inu ndinu kalata yocokela kwa Khristu yolembedwa ndi ife atumiki a Mulungu. Kalatayo si yolembedwa ndi inki, koma ndi mzimu wa Mulungu wamoyo. Si yolembedwa pa miyala koma m’mitima.*

4 Tingakambe zimenezi molimba mtima pamaso pa Mulungu kudzela mwa Khristu. 5 Sitingakambe kuti ndife oyenelela kwambili kugwila nchitoyi cifukwa ca mphamvu zathu ai, koma ndife oyenelela kwambili cifukwa ca Mulungu, 6 ndipo iye anationa kuti ndife oyenela kukhala atumiki a cipangano catsopano osati mwa malamulo olembedwa koma mwa mzimu. Pakuti malamulo olembedwa amapha, koma mzimu umapatsa munthu moyo.

7 Malamulo amene amabweletsa imfa, amenenso analembedwa pa miyala, anabwela ndi ulemelelo waukulu moti Aisiraeli sanakwanitse kuyang’anitsitsa nkhope ya Mose cifukwa inali kuwala ndi ulemelelo umene unatha patapita nthawi. 8 Kodi si ndiye kuti mzimu uyenela kupelekedwa ndi ulemelelo waukulu kuposa pamenepa? 9 Ngati malamulo oweluza anthu kuti alangidwe anapelekedwa ndi ulemelelo, ndiye kuti cilungamo ciyenela kupelekedwa ndi ulemelelo woposa pamenepo. 10 Ndipo ngakhale kuti malamulo olembedwa anapatsidwa ulemelelo, ulemelelo wake wacotsedwa cifukwa ulemelelo umene wabwela pambuyo pake ndi waukulu kuposa woyambawo. 11 Ngati malamulo olembedwa amene anatha patapita nthawi anapelekedwa ndi ulemelelo, ndiye kuti malamulo amene sadzatha adzakhala ndi ulemelelo waukulu kuposa pamenepo.

12 Popeza tili ndi ciyembekezo cimeneci, tili ndi ufulu waukulu wakulankhula. 13 Siticita zimene Mose anacita amene anaphimba nkhope yake ndi nsalu, kuti ana a Isiraeli asaone kutha kwa ulemelelo wosakhalitsawo. 14 Ndipo maganizo ao anacita khungu. Pakuti mpaka lelo, nsaluyo imakhalabe yophimba pamene akuwelenga cipangano cakale cija, cifukwa nsaluyo imacotsedwa kokha kudzela mwa Khristu. 15 Ndipo mpaka pano, akamawelenga zimene Mose analemba, mitima yao imakhalabe yophimba. 16 Koma munthu akasintha n’kutembenukila kwa Yehova, cophimbaco cimacotsedwa. 17 Yehova ndi Mzimu, ndipo pamene pali mzimu wa Yehova, pali ufulu. 18 Tonsefe tili ndi nkhope zosaphimba, ndipo tili monga magalasi oonela amene amaonetsa ulemelelo wa Yehova. Tikamaonetsa ulemelelo umenewo, timasintha kukhala ngati cifanizilo cake, ndipo timaonetsa ulemelelo woonjezeleka-onjezeleka* mofanana ndendende ndi mmene Yehova, amene ndi Mzimu,* watisinthila.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani