LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 2 Akorinto 6
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 2 Akorinto

      • Osagwilitsa nchito molakwa cisomo ca Mulungu (1, 2)

      • Paulo afotokoza utumiki wake (3-13)

      • Musamangidwe mu joko ndi wosakhulupilila (14-18)

2 Akorinto 6:1

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/15/2016, masa. 27-32

2 Akorinto 6:3

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 40

2 Akorinto 6:4

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 40

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    9/2016, masa. 18-19

2 Akorinto 6:11

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “Talankhula nanu moona mtima.”

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 56

2 Akorinto 6:12

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 56

2 Akorinto 6:13

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “tsegulani kwambili mitima yanu.”

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 56

    Galamuka!,

    na. 3 2020 tsa. 10

2 Akorinto 6:14

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 42

    Tikhalebe mu Cikondi ca Mulungu, masa. 134-135

    “m’Cikondi ca Mulungu,” tsa. 113

2 Akorinto 6:15

Mawu amunsi

  • *

    Kucokera ku liu la Ciheberi lotanthauza, “Wopanda Pake,” ndipo amalisewenzetsa pokamba za Satana.

  • *

    Kapena kuti, “munthu wokhulupilika.”

2 Akorinto 6:17

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Tikhalebe mu Cikondi ca Mulungu, tsa. 111

2 Akorinto 6:18

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Tikhalebe mu Cikondi ca Mulungu, tsa. 111

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
2 Akorinto 6:1-18

Kalata Yaciwiri kwa Akorinto

6 Pamene tikugwila nchito naye limodzi, tikukulimbikitsani kuti musalandile cisomo ca Mulungu n’kuphonya colinga ca cisomoco. 2 Cifukwa iye anati: “Pa nthawi yobvomelezeka ndinakumvela, ndipo pa tsiku la cipulumutso ndinakuthandiza.” Ndithudi, ino ndiyo nthawi yeniyeni yobvomelezeka. Lelo ndilo tsiku la cipulumutso.

3 Sitikucita ciliconse cokhumudwitsa, kuti anthu asaupeze cifukwa utumiki wathu . 4 Koma m’njila iliyonse, tikuonetsa kuti ndife atumiki a Mulungu. Tikucita zimenezi popilila mabvuto ambili, pokumana ndi masautso, pokhala opanda zinthu zofunikila, pokumana ndi zobvuta, 5 pomenyedwa, poikidwa m’ndende, pokumana ndi zipolowe, pogwila nchito mwakhama, posagona tulo, komanso posowa cakudya. 6 Tikucitanso zimenezi mwa kukhala oyela, acidziwitso , oleza mtima, okoma mtima, potsogoleledwa ndi mzimu woyela, poonetsa cikondi copanda cinyengo, 7 polankhula zoona, komanso pokhala ndi mphamvu ya Mulungu. Ndiponso tikucita zimenezi ponyamula zida zacilungamo kudzanja lamanja komanso lamanzele, 8 popatsidwa ulemelelo komanso ponyozedwa, poneneledwa zoipa komanso zabwino. Timaonedwa ngati anthu acinyengo koma ndife acilungamo, 9 ngati osadziwika koma ndife odziwika bwino, ngati kuti tikufa koma tikukhalabe ndi moyo, ngati olandila cilango koma osapita kukaphedwa, 10 ngati acisoni koma acimwemwe nthawi zonse, ngati osauka koma olemeletsa anthu oculuka, ngati anthu opanda kalikonse koma okhala ndi zinthu zonse.

11 Tatsegula pakamwa pathu kuti tilankhule ndi inu* Akorinto, ndipo tafutukula mtima wathu. 12 Ife sitimaumila pokuonetsani cikondi, koma inu mumaumila potionetsa cikondi. 13 N’cifukwa cake ndikulankhula nanu ngati ana anga, kuti inunso muzifutukula mitima yanu.*

14 Musamangidwe mu joko ndi anthu osakhulupilila, cifukwa ndinu osiyana. Kodi pali mgwilizano wanji pakati pa cilungamo ndi kuphwanya malamulo? Kapena pali kugwilizana kotani pakati pa kuwala ndi mdima? 15 Komanso pali mgwilizano wotani pakati pa Khristu ndi Beliyali?* Kapena munthu wokhulupilila* angagawane ciani ndi munthu wosakhulupilila? 16 Ndipo pali kugwilizana kotani pakati pa kacisi wa Mulungu ndi mafano? Pakuti ife ndife kacisi wa Mulungu wamoyo, monga mmene Mulungu anakambila kuti: “Ndidzakhala pakati pao komanso kuyenda pakati pao. Ndidzakhala Mulungu wao, ndipo iwo adzakhala anthu anga.” 17 “‘Conco cokani pakati pao ndipo mulekane nao,’ watelo Yehova. ‘Musakhudze cinthu codetsedwa,’” “‘ndipo ine ndidzakulandilani.’” 18 “‘Ndidzakhala atate wanu ndipo inu mudzakhala ana anga aamuna ndi aakazi,’ watelo Yehova Wamphamvuzonse.”

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani