LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 2 Akorinto 2
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 2 Akorinto

      • Colinga ca Paulo cakuti Akorinto asangalale (1-4)

      • Wocimwa akhululukidwa ndipo abwezeletsedwa (5-11)

      • Paula afika ku Torowa ndi ku Makedoniya (12, 13)

      • Utumiki uli ngati kuguba pa cionetselo coonetsa kupambana (14-17)

        • Siticita nao malonda mau a Mulungu (17)

2 Akorinto 2:7

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “kuti asamezedwe ndi cisoni.”

2 Akorinto 2:8

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    8/1/2013, tsa. 20

2 Akorinto 2:11

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “ku zolinga zake; mapulani ake.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
2 Akorinto 2:1-17

Kalata Yaciwiri kwa Akorinto

2 Pakuti ndatsimikiza mtima kuti ndisadzabwelenso kwa inu ndili wacisoni. 2 Ngati ndingakumvetseni cisoni nonsenu, palibe amene adzandisangalatsa kupatulapo inuyo amene ndakumvetsani cisoni. 3 Ndinalemba zonse zija kuti ndikadzafika kumeneko ndisadzakhale wacisoni cifukwa ca anthu amene ndiyenela kusangalala nao. Ndili ndi cikhulupililo kuti zimene zimandisangalatsa, zimasangalatsanso inu nonse. 4 Ndinakulembelani kalata ija ndili wosautsika, komanso ndikubvutika kwambili mumtima, kwinaku ndikugwetsanso misozi, osati kuti mucite cisoni, koma kuti mudziwe kuzama kwa cikondi cimene ndili naco pa inu.

5 Ngati wina wacita zinthu zomvetsa cisoni, sanamvetse ine cisoni, koma kwenikweni wamvetsa cisoni inu nonse. Komabe sindikufuna kukamba mwamphamvu za nkhani imeneyi. 6 Cidzudzulo copelekedwa ndi anthu ambili n’cokwanila kwa munthu wotelo. 7 Tsopano mukhululukileni mocokela pansi pa mtima ndipo mumutonthoze, kuti iye asakhale ndi cisoni copitilila malile n’kutaya* naco mtima. 8 Conco ndikukulimbikitsani kuti mum’tsimikizile kuti mumam’konda. 9 Ici ndiye cifukwa cakenso ndinakulembelani kuti ndidziwe ngati mumamvela pa zinthu zonse. 10 Ngati mwakhululukila munthu wina ciliconse, inenso ndimukhululukila. Ndipo ciliconse cimene ndakhululukila munthu (ngati cilipo cinthu cimeneco) ndatelo cifukwa ca inu pamaso pa Khristu, 11 kuti Satana asaticenjelele, pakuti ife sindife mbuli ku ziwembu zake.*

12 Tsopano nditafika ku Torowa kuti ndilengeze uthenga wabwino wonena za Khristu, komanso mwai wogwila nchito ya Ambuye utanditsegukila, 13 mtima wanga sunakhazikike cifukwa coti sindinamupeze m’bale wanga Tito. Conco ndinatsanzikana ndi abale kumeneko n’kupita ku Makedoniya.

14 Alemekezeke Mulungu amene nthawi zonse amatitsogolela pamodzi ndi Khristu, ngati kuti tikuguba pa cionetselo conyadila kupambana. Ndipo kupitila mwa ife, kapfungo konunkhila bwino kodziwa Mulungu kakufalikila konse-konse. 15 Pakuti kwa Mulungu ndife kapfungo kabwino konunkhila ka uthenga wabwino wa Khristu, kwa amene akupita ku cipulumutso komanso amene akupita kucionongeko. 16 Tsopano kwa amene akupita kukaonongedwa, ndife pfungo la imfa lotsogolela ku imfa. Koma kwa amene akupulumutsidwa, ndife kapfungo kabwino kotsogolela ku moyo. Ndipo ndani ali woyenela kugwila nchito imeneyi? 17 Ndife oyenelela. Pakuti siticita nao malonda mau a Mulungu monga mmene anthu ambili amacitila, koma timalalikila moona mtima monga otumidwa ndi Mulungu pamodzi ndi Khristu pamaso pa Mulungu.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani