LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • kr nkhani 30-31
  • Coonadi ca Ufumu—Kugaŵila Cakudya ca Kuuzimu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Coonadi ca Ufumu—Kugaŵila Cakudya ca Kuuzimu
  • Ufumu wa Mulungu Ukulamulila
  • Nkhani Zofanana
  • Motsogozela Phunzilo la Baibo Poseŵenzetsa Buku la “Kondwelani na Moyo Kwamuyaya!”
    Kondani Anthu Kuti Mupange Ophunzila
  • Thandizani Maphunzilo Anu a Baibo Kuti Akakhale Ophunzila Obatizika
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2021
  • Mmene Tingatsogozele Phunzilo la Baibo Lotsogolela Munthu ku Ubatizo—Gawo 2
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2020
  • Monga Mpingo, Thandizani Maphunzilo a Baibo Kupita Patsogolo Kuti Akabatizike
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2021
Onaninso Zina
Ufumu wa Mulungu Ukulamulila
kr nkhani 30-31
1. Akumvetsela uthenga wa m’Baibulo pa galamafoni ca m’ma 1930; 2. Phunzilo la Baibulo ku Switzerland

Kulamanzele: Mlongo ku Alabama, m’dziko la U.S.A., akumvetsela nkhani ya M’bale Rutherford imene inajambulidwa pa tepi ca kumapeto kwa zaka za m’ma 1930; kulamanja: ku Switzerland

CIGAWO 1

Coonadi ca Ufumu—Kugaŵila Cakudya ca Kuuzimu

YELEKEZELANI kuti mukuphunzila Baibulo ndi wophunzila Baibulo wanu. Nkhope yake ikuoneka yacimwemwe cifukwa cakuti wamvetsetsa mfundo ya palemba limene mwaŵelenga naye. Motsitsa mau, wophunzilayo akufunsa kuti, “Kodi mukutanthauza kuti Baibulo limaphunzitsa kuti tingakhale m’Paladaiso kwamuyaya pano padziko lapansi?” Mnzanu amene muli naye muutumiki akumwetulila ndi kuyankha kuti, “Izi n’zimene Baibulo limaphunzitsa.” Kenako wophunzilayo akugwedeza mutu, ndipo modabwa akunena kuti, “Izi n’zocititsa cidwi kwambili, ndipo sindinaphunzilepo zimenezi.” Ndiyeno inu mukukumbukila kuti milungu ingapo yapita, iye anakamba mau ofanana ndi amenewa pamene anadziŵa kuti dzina la Mulungu ndi Yehova.

Kodi zotelezi zinakucitikilamponi? Atumiki ambili a Mulungu zinawacitikilapo. Zocitika zotele zimatikumbutsa za mphatso ya mtengo wapatali imene tinapatsidwa. Mphatso imeneyi ndi coonadi cimene tinaphunzila. Komabe, kodi zinatheka bwanji kuti inuyo muphunzile coonadi cimeneci? M’cigawo cino tiphunzila yankho la funso limeneli. Njila imene anthu a Mulungu aphunzilila coonadi ndi umboni wakuti Ufumu wa Mulungu ndi weniweni. Kwa zaka zambili, Mfumu ya Ufumuwu, Yesu Kristu, yakhala ikuthandiza anthu a Mulungu kuphunzila coonadi.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani