LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • fg phunzilo 12 Mafunso. 1-5
  • Kodi Mungamuyandikile Bwanji Mulungu?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Mungamuyandikile Bwanji Mulungu?
  • Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Nkhani Zofanana
  • Yandikilani kwa Mulungu Kupitila M’pemphelo
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Mwayi Wa Pemphelo
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • Muyandikileni Mulungu Kupitila m’Pemphelo
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Kodi Mulungu Amamva Mapemphelo Athu?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2021
Onaninso Zina
Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
fg phunzilo 12 Mafunso. 1-5

PHUNZILO 12

Kodi Mungamuyandikile Bwanji Mulungu?

1. Kodi Mulungu amamva mapemphelo onse?

Munthu apemphela kwa Mulungu

Mulungu amafuna kuti anthu a mitundu yonse ayandikile kwa iye mwa kumapemphela. (Salimo 65:2) Komabe, iye samamva kapena kuti kulandila mapemphelo onse. Mwacitsanzo, Mulungu angatsekeleze mapemphelo a mwamuna amene amacitila nkhanza mkazi wake. (1 Petulo 3:7) Ndiponso, pamene Aisiraeli anapitiliza kucita zoipa, Mulungu sanamvele mapemphelo ao. N’zoonekelatu kuti, pemphelo ndi mwai wapadela kwambili. Komabe, Mulungu amalandila mapemphelo ngakhale a anthu ocimwa ngati io alapadi.​—Ŵelengani Yesaya 1:15; 55:7.

Tambani vidiyo Kodi Mulungu Amamvela Mapemphelo Onse?

2. Kodi tiyenela kupemphela bwanji?

Pemphelo ni mbali ya kulambila kwathu. Conco, tiyenela kupemphela cabe kwa Mlengi wathu, Yehova. (Mateyu 4:10; 6:9) Popeza ndife opanda ungwilo, tiyenelanso kupemphela m’dzina la Yesu cifukwa anafela macimo athu. (Yohane 14:6) Yehova samafuna kuti tizipeleka mapemphelo oloŵeza pamtima kapena olemba m’buku. Amafuna kuti tizipemphela kucokela pansi pa mtima.​—Ŵelengani Mateyu 6:7; Afilipi 4:6, 7.

Mlengi wathu amamva ngakhale mapemphelo a mumtima. (1 Samueli 1:12, 13) Iye amatiuza kuti tizipemphela nthawi iliyonse, monga kum’maŵa tikauka, popita kukagona, panthawi ya cakudya, ndi pamene takumana ndi mavuto.​—Ŵelengani Salimo 55:22; Mateyu 15:36.

3. N’cifukwa ciani Akristu amasonkhana pamodzi?

Anthu aŵelenga Baibo pamsonkhano wacikristu

Kuyandikila kwa Mulungu si cinthu copepuka cifukwa tikhala pakati pa anthu amene samakhulupilila Mulungu, ndipo amasuliza lonjezo lake lakuti adzabweletsa mtendele pa dziko lapansi. (2 Timoteyo 3:1, 4; 2 Petulo 3:3, 13) Mwa ici, timafunikila cilimbikitso ca olambila anzathu, ndipo naonso amafuna kuti tiziwalimbikitsa.​—Ŵelengani Aheberi 10:24, 25.

Kugwilizana ndi anthu amene amakonda Mulungu kumatithandiza kuti timuyandikile. Misonkhanoya Mboni za Yehova imapeleka mipata yabwino yakuti tilimbikitsidwe ndi cikhulupililo ca ena.​—Ŵelengani Aroma 1:11, 12.

4. Kodi mungamuyandikile bwanji Mulungu?

Munthu aŵelenga Baibo panthawi yopuma kunchitolabel

Mungamuyandikile Yehova mwa kusinkha-sinkha zimene mwaphunzila m’Mau ake. Ganizilani zimene mwaphunzila pa zocita zake, malangizo ake, ndi malonjezo ake. Pemphelo ndi kusinkha-sinkha kumatithandiza kuyamikila cikondi ca Mulungu ndi nzelu zake.​—Ŵelengani Yoswa 1:8; Salimo 1:1-3.

Mungayandikile Mulungu ngati mumam’dalila ndi kum’khulupilila. Koma cikhulupililo cili monga cinthu camoyo cimene cimafunika zakudya. Muyenela nthawi zonse kudyetsa cikhulupililo canu mwa kusinkha-sinkha zifukwa zimene zimakucititsani kukhala ndi cikhulupililo cimeneco.​—Ŵelengani Mateyu 4:4; Aheberi 11:1, 6.

5. Kodi kuyandikila Mulungu kungakuthandizeni bwanji?

Yehova amasamala anthu amene amam’konda. Angawachinjilize ku zilizonse zimene zingaononge cikhulupililo ndi ciyembekezo cao ca moyo wosatha. (Salimo 91:1, 2, 7-10) Iye amaticenjeza za njila zoipa zimene zingaononge thanzi lathu ndi kutilanda cimwemwe. Yehova amatiphunzitsa njila yabwino yotsatila pa umoyo wathu.​—Ŵelengani Salimo 73:27, 28; Yakobo 4:4, 8.

Mabwenzi asangalala pamodzi

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 17 m’buku lakuti Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani