LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • g19 na. 2 masa. 12-13
  • Citsogozo ca Anthu Acikulile N’cofunikila

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Citsogozo ca Anthu Acikulile N’cofunikila
  • Galamuka!—2019
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • KODI N’NDANI AFUNIKA KUPELEKA CITSOGOZO KWA ANA?
  • N’CIFUKWA CIANI CITSOGOZO CA ANTHU ACIKULILE N’COFUNIKA?
  • MMENE MUNGAPELEKELE CITSOGOZO KWA ANA ANU
  • Inu Makolo—Thandizani Ana Anu Kukonda Yehova
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
Galamuka!—2019
g19 na. 2 masa. 12-13
Wacikulile aonetsa kamtsikana mapikica ake akale

PHUNZILO 5

Citsogozo Ca Anthu Acikulile N’cofunikila

KODI N’NDANI AFUNIKA KUPELEKA CITSOGOZO KWA ANA?

Ana amafunikila citsogozo na malangizo ocokela kwa anthu acikulile mu umoyo wawo. Monga kholo, muli pamalo abwino kucita zimenezi, ndipo ni udindo wanu. Komabe, anthu ena acikulile angakuthandizileni kulangiza ana anu.

N’CIFUKWA CIANI CITSOGOZO CA ANTHU ACIKULILE N’COFUNIKA?

M’maiko ambili, anthu acicepele saceza kwambili na acikulile. Ganizilani izi:

  • Ana amathela nthawi yoculuka ku sukulu, kumene ana ndiwo amakhalako ambili kuposa matica ngakhale acikulile.

  • Acinyamata ena akakomboka ku sukulu, amapeza kuti makolo onse aŵili kulibe ku nyumba, mwina cifukwa cakuti onse amapita ku nchito.

  • Kafukufuku wina anapeza kuti ku America, ana a zaka pakati pa 8 na 12, amathela maola pafupifupi 6 tsiku lililonse, pa zosangalatsa za pa zipangizo zamakono.a

Buku lakuti Hold On to Your Kids limati: “Acicepele masiku ano amakonda kufunsila kwa  . . . acicepele anzawo malangizo, citsogozo, komanso kufuna kutengela zitsanzo zawo, m’malo mofunsila kwa amayi awo, atate awo, aphunzitsi, kapena anthu ena acikulile.”

MMENE MUNGAPELEKELE CITSOGOZO KWA ANA ANU

Muzipeza nthawi yoceza nawo.

MFUNDO YA M’BAIBO: “Phunzitsa mwana m’njila yomuyenelela. Ngakhale akadzakalamba sadzapatukamo.”—Miyambo 22:6.

Mwacibadwa, ana amafuna citsogozo ca makolo awo. Akatswili amakamba kuti acicepele azaka pakati pa 13 na 19, amaona kuti citsogozo ca makolo awo n’cofunika ngako kuposa ca acicepele anzawo. “Makolo amakhalabe othandiza kwambili kuti ana awo akhale na maganizo, komanso makhalidwe abwino kuyambila ali aang’ono, mpaka m’zaka zaunyamata.” Izi n’zimene analemba Dr. Laurence Steinberg m’buku lakuti, You and Your Adolescent. Iye anawonjezela kuti: “Acicepele amafuna kumvela malingalilo a imwe makolo. Ndiponso amafuna kumvetsela zimene mungakambe, ngakhale kuti si nthawi zonse pamene angavomeleze poyela zimenezi, kapena kugwilizana na zonse zimene mungaŵauze.”

Mwacibadwa, ana amafuna citsogozo ca imwe makolo. Conco, athandizeni mwa kuwapatsa citsogozo canu. Pezani nthawi yoceza ndi ana anu, na kuŵauzako malingalilo anu pa nkhani zina. Mungaŵauzenso zimene mumaona kuti n’zofunika, na zimene mwapitamo mu umoyo wanu.

Apezeleni woŵathandiza.

MFUNDO YA M’BAIBO: “Munthu woyenda ndi anthu anzelu adzakhala wanzelu.”—Miyambo 13:20.

Kodi mungaganizileko munthu wina, wamakhalidwe abwino amene angakhalenso citsanzo cabwino kwa mwana wanu? Bwanji osakonza zakuti munthuyo azicezako na mwana wanu? Koma sititanthuza kuti mukam’tulile udindo wanu monga kholo ayi. Munthu wacikulile amene mumam’dalila kuti sangasokoneze mwana wanu, angakuthandizeni kupeleka citsogozo. Baibo imaonetsa kuti ngakhale pamene Timoteyo anakula, anali kupindulabe kwambili na mgwilizano umene anali nawo na mtumwi Paulo, ndipo nayenso Paulo anali kupindula.—Afilipi 2:20, 22.

Masiku ano, anthu m’mabanja ambili sakhalila pamodzi. Mwina n’cifukwa cakuti azimbuye, azimalume, anti, komanso acibale ena amakhala kwina. Ngati ni mmene zinthu zilili kwa inu, yesetsani kupezela ana anu mipata yoceza na anthu acikulile amene ali na makhalidwe abwino, amene mungakonde kuti ana anu akhale nawo.

a Kafukufuku ameneyu anapezanso kuti acicepele a zaka pakati pa 13 na 19, amathela maola pafupifupi 9 tsiku lililonse, pa zosangalatsa za pa zipangizo zamakono. Pakafukufuku ameneyo, sanaphatikizepo nthawi imene acinyamatawa amathela pa intaneti ya ku sukulu, komanso pocita homuweki.

Wacikulile aonetsa kamtsikana mapikica ake akale

APHUNZITSENI AKALI AANG’ONO

Mwana amene amapempha citsogozo kwa anthu acikulile, akakula amacita zinthu mwanzelu, ndiponso amakhala wokhwima m’maganizo

Aphunzitseni mwa Citsanzo Canu

  • Kodi ndine citsanzo cabwino kwa ana anga?

  • Kodi ana anga amaona kuti na ine nimafunsila malangizo kwa anthu acikulile?

  • Kodi nimaonetsa ana anga kuti ni ofunika kwa ine, mwa kupatula nthawi yoceza nawo?

Zimene Makolo Ena Anacita . . .

“Nthawi zina pamene nili mkati mocita zinthu zina, mwana wanga wamkazi amabwela kuti akambe na ine. Ndipo nimayesetsa kum’patsa mpata kuti akambe. Ngati nili bize kwambili nimamuuza kuti aniyembekezeko, kuti nimumvetsele bwino-bwino pamene azikamba. Ine na mkazi wanga timayesetsa kukhala zitsanzo zabwino, kuti mwana wathu nayenso aziona kuti nafenso timatsatila mfundo zimene timam’phunzitsa.”—David.

“Pamene mwana wathu wamkazi anabadwa, ine na amuna anga tinakambilana kuti niyambe naima nchito, kuti ine nizithandiza kulela mwana wathu. Ndipo sinidziimba mlandu kucita zimenezi. Monga makolo, n’cinthu cofunika maningi kupatula nthawi yoceza na ana athu. Kucita zimenezi kudzaŵathandiza kulandila citsogozo cabwino mu umoyo wawo. Ndipo kuceza na mwana wanu kumaonetsa kuti mumam’konda kwambili.”—Lisa.

KUCEZA NA ANTHU ACIKULILE

“Ana anga akulila pa nyumba pamene pali anthu acikulile osiyana-siyana. Ndipo izi zaŵathandiza kuphunzila zinthu pa zocitika mu umoyo wa anthu ena. Mwacitsanzo, iwo anadabwa pamene ambuye anga aakazi anaŵauza kuti pamene anali kamtsikana, banja lawo linali loyamba kukhala na nyumba ya malaiti. Anaŵauzanso kuti anthu a m’dela lawo anali kubwela na kuimilila m’khichini kuonelela pamene ayatsa na kuzimya malaiti. Nkhaniyi inaonetsa ana anga mmene umoyo unalili kumbuyoko. Ndipo nkhani zimene anamvetsela kwa ambuya, zinaŵathandizanso kuwalemekeza na kulemekezanso anthu ena acikulile. Ngati ana aceza kwambili na acikulile kuposa anzawo, amaphunzila zambili kwa acikulile.”—Maranda.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani