LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w15 7/15 tsa. 32
  • Kodi Mukumbukila?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Mukumbukila?
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhani Zofanana
  • Nkhalango
    Galamuka!—2023
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
w15 7/15 tsa. 32
Nkhalango ya Biriya ya ku Galileya

Nkhalango ya Biriya ya ku Galileya (pansipa)

Kodi Mukumbukila?

Kodi ku Isiraeli wakale kunali nkhalango monga mmene Baibulo limanenela?

BAIBULO limafotokoza kuti madela ena a Dziko Lolonjezedwa anali ndi nkhalango zoŵilila. (1 Maf. 10:27; Yos. 17:15, 18) Anthu ena akamaona malo aakulu amene alibe mitengo masiku ano, amakaikila ngati kunalidi nkhalango.

Zipatso za mtengo wamkuyu

Zipatso za mtengo wamkuyu

Buku lina limati: “Kale ku Isiraeli kunali nkhalango zikuluzikulu kusiyana ndi masiku ano.” (Life in Biblical Israel) Nkhalango zimenezi zinali ndi mitengo ikuluikulu ya paini, oki ndi telebeti. Mitengo ya mkuyu inali kupezekanso m’cigawo ca Sefela, malo amene anali pakati pa mapili ndi nyanja ya Mediterranean.

Buku linanso limakamba kuti madela ena ku Isiraeli kulibiletu mitengo masiku ano. N’cifukwa ciani? Bukuli limafotoza kuti zimenezi zakhala zikucitika mwapang’onopang’ono. Limati: “Anthu akhala akudula mitengo makamaka kuti alambule malo olimapo ndi odyetsela ziŵeto, komanso kuti apezeko zomangila ndi nkhuni.”—Plants of the Bible.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani