LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp17 na. 4 masa. 4-7
  • Zimene Baibo Imakamba pa Nkhani ya Moyo na Imfa

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Zimene Baibo Imakamba pa Nkhani ya Moyo na Imfa
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • BAIBO IPELEKA YANKHO LA ZOONA
  • CIPHUNZITSO CACIKUNJA CIFALIKILA
  • “COONADI CIDZAKUMASULANI”
  • Kodi Akufa Ali Kuti?
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
wp17 na. 4 masa. 4-7
Mtembo m’manda

NKHANI YA PACIKUTO | KODI BAIBO IMATI CIANI PA NKHANI YA MOYO NA IMFA?

Zimene Baibo Imakamba pa Nkhani ya Moyo na Imfa

Tikaŵelenga nkhani yokamba za cilengedwe m’buku ya m’Baibo ya Genesis, timaphunzila kuti Mulungu anauza munthu woyamba, Adamu, kuti: “Zipatso za mtengo uliwonse wa m’mundamu uzidya ndithu. Koma usadye zipatso za mtengo wodziŵitsa cabwino ndi coipa. Cifukwa tsiku limene udzadya, udzafa ndithu.” (Genesis 2:16, 17) Mau awa amaonetsa bwino kuti Adamu akanamvela lamulo la Mulungu, sembe sanafe. Akanapitiliza kukhala m’munda wa Edeni.

Adamu ndi Hava okalamba

N’zacisoni kuti m’malo mosankha kumvela lamulo la Mulungu kuti akhale na moyo kwamuyaya, Adamu anasankha kusamvela. Anadya cipatso coletsedwa cimene mkazi wake, Hava, anam’patsa. (Genesis 3:1-6) Zotulukapo za kusamvela kumeneko zimatikhudza mpaka lelo. Pankhani imeneyi, mtumwi Paulo anakamba kuti: ‘Ucimo unaloŵa m’dziko kudzela mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzela mwa ucimo, imfayo n’kufalikila kwa anthu onse cifukwa onse anacimwa.’ (Aroma 5:12) “Munthu mmodzi” ameneyo ni Adamu. Koma kodi ucimo unali ciani? Nanga unatsogolela bwanji ku imfa?

Adamu anaphwanya lamulo la Mulungu mwadala. Zimene anacitazi ni chimo. (1 Yohane 3:4) Ndipo cilango ca ucimo ni imfa, monga mmene Mulungu anauzila Adamu. Zikanakhala kuti Adamu na mbadwa zake za m’tsogolo anamvela lamulo la Mulungu, sembe iwo sanacimwe na kulaŵa imfa. Mulungu sanapange anthu kuti azifa, koma kuti akhale na moyo kwamuyaya.

Palibe angatsutse kuti imfa sinafalikile kwa “anthu onse,” monga mmene Baibo imakambila. Koma kodi pali cinacake m’thupi mwathu cimene cimapitiliza kukhala na moyo tikafa? Ambili angayankhe kuti inde, cinacake m’thupi mwathu—cochedwa mzimu—sicimafa. Komabe, zimenezi zingatanthauze kuti Mulungu ananamiza Adamu. N’cifukwa ciani takamba conco? Cifukwa ngati cinacake m’thupi mwathu cimacoka tikafa na kukakhala ndi moyo kwinakwake, sembe imfa sikanakhala cilango ca ucimo, monga mmene Mulungu anakambila. Baibo imati: “N’zosatheka kuti Mulungu aname.” (Aheberi 6:18) Zoona zake n’zakuti Satana ndiye anakamba bodza pamene anauza Hava kuti: “Kufa simudzafa ayi.”—Genesis 3:4.

Izi zibweletsa funso lakuti, Ngati ciphunzitso cakuti mzimu sukufa n’cabodza, n’ciani cimacitika kweni-kweni munthu akafa?

BAIBO IPELEKA YANKHO LA ZOONA

Nkhani yokamba za cilengedwe m’buku la Genesis limati: “Yehova Mulungu anaumba munthu kucokela kufumbi lapansi, ndipo anauzila mpweya wa moyo m’mphuno mwake, munthuyo n’kukhala wamoyo.” Mau akuti “wamoyo” anamasulidwa kucokela ku liu la Ciheberi lakuti ne’phesh, limene limatanthauza “colengedwa copuma.”—Genesis 2:7, nwt-E mau amunsi.

Apa Baibo imaonetsa bwino kuti anthu sanalengedwe ndi mzimu umene sukufa iyai. Komabe, munthu aliyense ni ‘moyo.’ Ndiye cifukwa cake, ngati mwafufuza m’Baibo, simudzapezamo vesi imene pali mau akuti “mzimu wosafa.”

Popeza Baibo sikamba kuti anthu ali ndi cinacake m’thupi mwawo cimene ena amati mzimu umene sukufa, n’cifukwa ciani machechi ambili amaphunzitsa zimenezi? Kuti tipeze yankho, tifunika kuganizila za dziko la Iguputo wakale.

CIPHUNZITSO CACIKUNJA CIFALIKILA

Herodotus, katswili wacigiriki wolemba mbili yakale wa m’zaka za m’ma 400 B.C.E., anakamba kuti Aiguputo ndiwo anali “anthu oyamba kuikila kumbuyo ciphunzitso cakuti mzimu wa munthu sukufa.” Nawonso Ababulo akale anacilikiza zakuti mzimu sukufa. Podzafika m’nthawi imene Alexander Wamkulu anagonjetsa cigawo ca Middle East mu 332 B.C.E., akatswili acigiriki anali atafalitsa ciphunzitso cimeneci, ndipo m’kupita kwa nthawi cinafalikila mu Ufumu wa Girisi.

M’Baibo simudzapezamo mau akuti “mzimu wosafa”

M’zaka 100 zoyambilila, magulu aŵili ochuka aciyuda, Aesene ndi Afarisi, anali kuphunzitsa kuti munthu akafa, mzimu wake umapitiliza kukhala na moyo. Buku yakuti The Jewish Encyclopedia inati: “Ayuda anayamba kukhulupilila kuti mzimu sukufa pambuyo potengela maganizo a Agiriki, makamaka cifukwa ca ciphunzitso ca Plato.” Nayenso Josephus, wolemba mbili waciyuda wa m’zaka 100 zoyambilila, anakamba kuti ciphunzitso cimeneci si ca m’Malemba Oyela, koma “ni cikhulupililo ca Agiriki,” cimene anaona kuti n’cozikidwa pa nthano zabodza.

Cikhalidwe ca Agiriki citafala kwambili, anthu odzicha Akhristu, nawonso anatengela ciphunzitso cacikunja cimeneci. Wolemba mbili yakale dzina lake Jona Lendering anakamba kuti “maganizo a Plato akuti mzimu wathu unali kukhala m’dziko labwino koma tsopano ukukhala kumalo osayenela, anapangitsa kuti kukhale kosavuta kusanganiza ciphunzitso ca Plato ndi Cikhristu.” Conco, ciphunzitso cacikunja cakuti mzimu sukufa cinaloŵa mu “Cikhristu,” ndipo cinakhala mbali yaikulu ya zikhulupililo za machechi.

“COONADI CIDZAKUMASULANI”

M’zaka 100 zoyambilila, mtumwi Paulo anacenjeza kuti: “Mau ouzilidwa amanenadi kuti m’nthawi zam’tsogolo, ena adzagwa pa cikhulupililo, cifukwa comvetsela mau ouzilidwa omwe ndi osoceletsa, ndiponso ziphunzitso za ziŵanda.” (1 Timoteyo 4:1) Izi zinacitikadi. Ciphunzitso cakuti mzimu sukufa n’cimodzi mwa “ziphunzitso za ziŵanda.” Si cocokela m’Baibo, koma cinayambila ku zipembedzo zakale zacikunja ndi nzelu za anthu.

Ndife okondwa kuti Yesu anati: “Mudzadziŵa coonadi, ndipo coonadi cidzakumasulani.” (Yohane 8:32) Kudziŵa coonadi colongosoka copezeka m’Baibo kumatimasula ku ziphunzitso zosalemekeza Mulungu, ndi ku miyambo ya zipembedzo zambili padziko lapansi. Kuonjezela apo, coonadi ca m’Mau a Mulungu cimatimasula ku zikhulupililo ndi zamatsenga zogwilizana ndi imfa.—Onani bokosi yakuti “Kodi Akufa Ali Kuti?”

Mlengi wathu sanalenge anthu kuti azikhala zaka 70 kapena 80 padziko lapansi, ndiyeno n’kupita kukakhala kwamuyaya kumalo ena ake. Colinga cake ca poyamba cinali cakuti anthu akhale kwamuyaya pano padziko lapansi monga ana ake omvela. Colinga cake cacikulu cimeneci cimaonetsa cikondi ca Mulungu pa anthu, ndipo sicidzalephela olo pang’ono. (Malaki 3:6) Wamasalimo anauzilidwa kulemba kuti: “Olungama adzalandila dziko lapansi, ndipo adzakhala mmenemo kwamuyaya.”—Salimo 37:29.

Kuti mudziŵe zambili zokhudza zimene Baibo imakamba pa nkhani ya moyo na imfa, onani nkhani 6 m’buku yakuti Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni yofalitsiwa na Mboni za Yehova. Buku imeneyi ipezekanso pa webusaiti ya www.jw.org, kapena mungaunike QR khodi iyi.

Kodi N’zotheka Anthu Kukhala Kwamuyaya?

Zaka zingapo zapitazo, akatswili ofufuza zinthu anapeza zomela zina za m’nyanja. Iwo amakhulupilila kuti zomelazo zakhalako zaka masauzande ambili, mwina kuposa camoyo ciliconse padziko lapansi. Zomelazo zili m’gulu lochedwa Posidonia oceanica, mtundu wa maudzu a m’nyanja amene anamela kwambili pansi pa nyanja ya Mediterranean, pakati pa dziko la Spain ndi Cyprus.

Ngati zomela zingakhale na moyo zaka zonsezo, nanga bwanji anthu? Asayansi amene amafufuza za ukalamba amakhulupilila kuti angathe kutalikitsa moyo wa munthu. Mwacitsanzo, buku lina limakamba kuti “asayansi apita patsogolo kwambili m’kafuku-fuku wawo” pa nkhani imeneyi. N’zokaikitsa kuti kupita patsogolo kwa sayansi kungathandize kutalikitsa moyo wa munthu.

Ngakhale n’conco, ciyembekezo cokhala ndi moyo kwamuyaya sicidalila sayansi. Baibo imakamba za Mlengi wathu, Yehova Mulungu, kuti: “Inu ndinu kasupe wa moyo.” (Salimo 36:9) Pokamba za iye, Yesu Khristu anapemphela kuti: “Pakuti moyo wosatha adzaupeza akamaphunzila ndi kudziŵa za inu, Mulungu yekhayo amene ali woona, ndi za Yesu Khristu, amene inu munamutuma.” (Yohane 17:3) Kukamba zoona, tidzalandila madalitso osatha ngati ticita khama kuti tidziŵe Yehova Mulungu na Mwana wake, Yesu Khristu, komanso kucita zinthu zowakondweletsa.

Maudzu a m’nyanja

Akatswili ofufuza zinthu amakhulupilila kuti zomela izi za mtundu wa maudzu zakhalako zaka masauzande ambili

KODI AKUFA ALI KUTI?

Yesu aukitsa Lazaro

Kuyankha mwacidule, Baibo imakamba kuti akufa ali kumanda, kuyembekezela kuukitsidwa. (Yohane 5:28, 29) Kumeneko iwo savutika kapena kumvela kuŵaŵa kulikonse, cifukwa “akufa sadziŵa ciliconse.” (Mlaliki 9:5) Pophunzitsa, Yesu anayelekezela imfa ndi tulo tofa nato. (Yohane 11:11-14) Conco, palibe cifukwa coopela anthu amene ali m’tulo twa imfa, kapena kuwakondweletsa mwa kuwapelekela mphatso. Iwo sangatithandize kapena kutivulaza, cifukwa ku Manda “kulibe kugwila nchito, kuganiza zocita, kudziŵa zinthu, kapena nzelu.” (Mlaliki 9:10) Komabe, Mulungu adzathetselatu imfa mwa kuukitsa akufa.—1 Akorinto 15:26, 55; Chivumbulutso 21:4.

Cifukwa Cake Mungakhulupilile Zimene Baibo Imakamba

Tingakhulupilile kuti zimene Baibo imakamba n’zoona. Cifukwa ciani? Onani zifukwa zotsatilazi:

  • Kolembela ndi kabotolo koikamo inki

    Anailemba ni Wapadela: Baibo ili na mabuku okwana 66. Amene analemba mabukuwo ni amuna 40, ndipo anatenga zaka zoposa 1,600, kuyambila mu 1513 B.C.E. mpaka mu 98 C.E. Komabe, nkhani zake n’zogwilizana ndi zomveka bwino. Izi zionetsa kuti Mlembi wake weni-weni ni Mulungu wamphamvuzonse. Iye anauzila amunawo kulemba maganizo ake.

  • Cipilala

    Imakamba Zoona pa Mbili Yakale: Zocitika zolembewa m’Baibo zigwilizana kwambili na mbili yakale yotsimikizika. Buku yakuti A Lawyer Examines the Bible inati: “Nkhani zacikondi, nthano, ndi maumboni abodza, zimalembedwa mosamala kwambili kuti zigwilizane ndi zocitika komanso nthawi ya kudela linalake, . . . koma nkhani za m’Baibo zimachula ndendende deti ndi malo kumene zinthuzo zinacitikila.”

  • Atomu

    Imakamba Zoona pa Nkhani za Sayansi: Baibo si buku ya sayansi. Koma ikamakamba za sayansi, imakamba zoona ndipo mfundo zake zinali zotsogola kwambili asayansi asanazitulukile. Mwacitsanzo, Levitiko macaputa 13 na 14 afotokoza malamulo amene anapatsidwa kwa Aisiraeli okamba za ukhondo na kupatula anthu odwala matenda oyambukila. Malamulowo anapelekedwa anthu akalibe kudziŵa ciliconse pankhani ya tuzilombo toyambitsa matenda komanso matenda oyambukila. Baibo imakambanso kuti dziko lapansi ni lozungulila ndipo lili m’malele. Asayansi sanali kudziŵa zeni-zeni pankhaniyi. Anadziŵa izi pambuyo pa zaka zambili.—Yobu 26:7; Yesaya 40:22.

Izi n’zifukwa zocepa cabe zotsimikizila kuti Baibo imakamba zoona pamene imati: “Malemba onse anauzilidwa ndi Mulungu, ndipo ndi opindulitsa pa kuphunzitsa, kudzudzula, [na] kuongola zinthu.”—2 Timoteyo 3:16.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani