LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 12/14 tsa. 6
  • Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
km 12/14 tsa. 6

Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki

Tidzakambilana mafunso otsatilawa pa Sukulu ya Ulaliki mkati mwa mlungu wa December 29, 2014.

  1. Kodi lamulo la pa Deuteronomo 14:1 loletsa kudzicekaceka pa nthawi yolila malilo timaliona bwanji? [Nov. 3, w04 9/15 tsa. 27 ndime 5]

  2. N’cifukwa ciani Mulungu analamula mafumu Aciisiraeli kuti azikopela buku la Cilamulo ca Mulungu ndi ‘kuliŵelenga masiku onse a moyo wao’? (Deut. 17:18-20) [Nov. 3, w02 6/15 tsa. 12 ndime 4]

  3. N’cifukwa ciani Baibulo limanena kuti “usamange ng’ombe ndi bulu kuti uzilimitse pamodzi,” ndipo Akristu angatsatile bwanji lamulo limeneli? (Deut. 22:10) [Nov. 10, w03 10/15 tsa. 32]

  4. N’cifukwa ciani Mulungu anali kuletsa munthu kulanda mnzake “mphelo kapena mwala wopelela monga cikole”? (Deut. 24:6) [Nov. 17, w04 9/15 tsa. 26 ndime 3]

  5. Kodi Aisiraeli anafunika kumvela Mulungu motani, nanga n’ciani cifunika kutilimbikitsa kutumikila Yehova? (Deut. 28:47) [Nov. 24, w10 9/15 tsa. 8 ndime 4]

  6. Kodi lemba la Deuteronomo 30:19, 20 limachula mfundo zitatu ziti zofunika kwambili kuti munthu akhalebe ndi moyo? [Nov. 24, w10 2/15 tsa. 28 ndime 17]

  7. Kodi tifunika kuchula mokweza mau onse a m’Baibulo kuyambila Genesis mpaka Chivumbulutso tikamaŵelenga? Fotokozani. (Yos. 1:8) [Dec. 8, w13 4/15 tsa. 7 ndime 4]

  8. Kodi “kalonga wa gulu lankhondo la Yehova” wochulidwa pa Yoswa 5:14, 15 ndani? Nanga nkhani imeneyi imatilimbikitsa bwanji? [Dec. 8, w04 12/1 tsa. 9 ndime 2]

  9. N’ciani cinacititsa kuti Akani acimwe? Nanga ife tingaphunzilepo ciani pa citsanzo cake coipa? (Yos. 7:20, 21) [Dec. 15, w10 4/15 tsa. 20-21 ndime 2, 5]

  10. Kodi citsanzo ca Kalebe cimatilimbikitsa bwanji masiku ano? (Yos. 14:10-13) [Dec. 29, w04 12/1 tsa. 12 ndime 2]

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani