LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w24 April tsa. 32
  • Anthu Auzimu Amapanga Zisankho Zanzelu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Anthu Auzimu Amapanga Zisankho Zanzelu
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2024
  • Nkhani Zofanana
  • Yakobo Analandila Coloŵa
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Mafunso Ocokela Kwa Oŵelenga
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2017
  • Ana Amapasa Osiyana
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Yakobo na Esau Akhalanso Pamtendele
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2024
w24 April tsa. 32

ZIMENE MUNGACITE PA PHUNZILO LA INU MWINI

Anthu Auzimu Amapanga Zisankho Zanzelu

Ŵelengani Genesis 25:​29-34 kuti muone ngati Esau na Yakobo anapanga zisankho zanzelu.

Kumbani mozamilapo kuti mumvetse nkhani yonse. Kodi zinthu zinali bwanji izi zisanacitike? (Gen. 25:​20-28) Nanga n’ciyani cinacitika pambuyo pake?—Gen. 27:​1-46.

Kumbani mozamilapo kuti mumvetse mmene zinthu zinali kucitikila pa nthawiyo. Ni mwayi wapadela uti, komanso ni maudindo ati amene mwana woyamba kubadwa anali kukhala nawo?—Gen. 18:​18, 19; w10 5/1 13.

  • Kodi munthu anayenela kukhala woyamba kubadwa kuti akhale mu mzele wobadwila Mesiya? (w17.12 14-15)

Pezani maphunzilo amene alipo na kuwaseŵenzetsa. N’cifukwa ciyani Yakobo anaona mwayi wokhala woyamba kubadwa kuti ni wamtengo wapatali kuposa mmene Esau anauonela? (Aheb. 12:​16, 17; w03 10/15 28-29) Kodi Yehova anali kuwaona bwanji anthu aŵili a pacibale amenewa? Ndipo n’cifukwa ciyani? (Mal. 1:​2, 3) Kodi Esau akanawongolela pati kuti apange zisankho zanzelu?

  • Dzifunseni kuti, ‘Kodi ningaonetse bwanji kuti nimayamikila zinthu zauzimu m’zocita zanga mlungu uliwonse?’ Mwa citsanzo, ‘kodi nimapatula tsiku komanso nthawi yokwanila yocita kulambila kwa pabanja?’

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani