LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • g20 na. 1 masa. 14-15
  • N’zotheka Kukhala na Umoyo Wopanda Nkhawa

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • N’zotheka Kukhala na Umoyo Wopanda Nkhawa
  • Galamuka!—2020
  • Nkhani Zofanana
  • Zamkati
    Galamuka!—2020
  • Mu Ufumu wa Mulungu, pa Dziko “Padzakhala Mtendele Woculuka”
    Galamuka!—2019
  • Zimene Mungacite kuti Muthane na Nkhawa
    Galamuka!—2020
  • Kodi Muli na Nkhawa?
    Galamuka!—2020
Onaninso Zina
Galamuka!—2020
g20 na. 1 masa. 14-15
Kamnyamata ndi atate ake akuseŵela m’mafunde apa nyanja, pamene amayi ndi ana aakazi atamba mokondwa ku mbali kwa nyanja.

PEZANI THANDIZO PA NKHAWA ZANU

N’zotheka Kukhala na Umoyo Wopanda Nkhawa

Nzelu zopezeka m’Baibo zingatithandize kupewa nkhawa zambili zosafunikila. Pa ife tekha sitingakwanitse kuthetsa zinthu zonse zimene zimatibweletsela nkhawa mu umoyo wathu. Koma Mlengi wathu angakwanitse. Iye anasankha munthu wina kuti atithandize. Munthuyo ni Yesu Khristu. Posacedwa, iye adzacita zinthu zambili zabwino pa dziko lonse la pansi, kuposa zimene anacita pamene anali pa dziko monga munthu. Mwacitsanzo:

YESU ADZACILITSA ODWALA MONGA MMENE ANACITILA ALI PA DZIKO LAPANSI.

“Anthu anamubweletsela onse amene sanali kumva bwino m’thupi, amene anali kuvutika ndi matenda . . . , ndipo iye anawacilitsa.”​—MATEYU 4:24.

YESU ADZATHANDIZA ANTHU ONSE KUKHALA NA NYUMBA KOMANSO CAKUDYA.

“Iwo [olamulilidwa na Khristu] adzamanga nyumba n’kukhalamo. Adzabzala minda ya mpesa n’kudya zipatso zake. Sadzamanga wina n’kukhalamo. Sadzabzala wina n’kudya.”​—YESAYA 65:21, 22.

ULAMULILO WA YESU UDZABWELETSA MTENDELE NA CITETEZO PA DZIKO LONSE.

“M’masiku ake, wolungama adzaphuka, ndipo padzakhala mtendele woculuka kwa nthawi yonse pamene mwezi udzakhalepo. Ndipo adzakhala ndi anthu omugonjela kucokela kunyanja kukafika kunyanja, komanso kucokela ku Mtsinje kukafika kumalekezelo a dziko lapansi. . . . Ndipo adani ake adzabwila fumbi.”​—SALIMO 72:7-9.

YESU ADZATHETSA KUPANDA CILUNGAMO.

“Adzamvela cisoni munthu wonyozeka ndi wosauka, ndipo adzapulumutsa miyoyo ya anthu osauka. Adzawombola miyoyo yawo ku cipsinjo ndi ciwawa.”​—SALIMO 72:13, 14.

YESU ADZATHETSA MAVUTO NA IMFA.

“Imfa sidzakhalaponso. Sipadzakhalanso kulila, kapena kubuula, ngakhale kupweteka.”​—CHIVUMBULUTSO 21:4.

“NTHAWI YAPADELA KOMANSO YOVUTA”

—Mohamed S. Younis,mkonzi wamkulu wa magazini yochedwa Gallup anati: “Anthu m’dzikoli ni opanikizika maganizo kwambili, a nkhawa, okhumudwa, komanso ali na zoŵaŵa zambili kuposa kale lonse.”

N’cifukwa ciani ambili ali na nkhawa? Baibo imapeleka yankho yomveka bwino. Pa 2 Timoteyo 3:1 imati: “Masiku otsiliza adzakhala nthawi yapadela komanso yovuta.” Kenako, Baibo imafotokoza cifukwa cake anthu ambili amavutika na nkhawa, mwa kuchula makhalidwe oipa amene anthu adzakhala nawo. Ena mwa makhalidwe amenewa ni dyela, kudzitukumula, cinyengo cacipembedzo, nkhanza, kusakonda acibale, komanso kusadziletsa. (2 Timoteyo 3:2-5) Masiku otsiliza adzatha pamene Yesu Khristu adzakhala na mphamvu zonse zolamulila dziko lapansi monga Mfumu ya Ufumu wa Mulungu, umene ni boma lakumwamba.—Danieli 2:44.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani