LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • my nkhani 11
  • Utawaleza Woyamba

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Utawaleza Woyamba
  • Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Anthu 8 Anapulumuka na Kulowa m’Dziko Latsopano
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Kutengapo Phunzilo pa Zimene Zinacitika Kumbuyo
    Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • Cigumula ca Nowa—Ndani Anamvetsela? Ndani Sanamvetsele?
    Mvetselani kwa Mulungu Kuti Mukhale ndi Moyo Wamuyaya
  • Anam’sunga “Pomupulumutsa Pamodzi ndi Anthu Ena 7”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
Onaninso Zina
Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
my nkhani 11

Nkhani 11

Utawaleza Woyamba

KODI udziŵa cinthu coyamba cimene Nowa anacita pamene iye ndi banja lake anacoka m’cingalawa? Anapeleka nsembe kapena kuti mphatso kwa Mulungu. Ona mmene iye acitila zimenezi pacithunzi-thunzi apa. Nowa anapeleka nyama zimenezi monga mphatso kuti aonge zikomo kwa Mulungu cifukwa copulumutsa banja lake pa cigumula.

Kodi uganiza kuti Yehova analandila nsembe imeneyi? Inde, anailandila. Conco, analonjeza Nowa kuti sadzaononganso dziko ndi Cigumula.

Patapita kanthawi, madzi onse anauma, ndipo Nowa ndi banja lake anatuluka m’cingalawa ndi kuyamba moyo watsopano. Mulungu anawadalitsa ndipo anawauza kuti: ‘Mubalane, muculuke mudzaze dziko lapansi.’

Koma m’kupita kwa nthawi, anthu akanamvela za cigumula, akanacita mantha kuti cigumula cingacitikenso. Conco Mulungu anapatsa anthu cinthu cina cowakumbutsa lonjezo lakuti sadzaononganso dziko lonse lapansi ndi cigumula. Kodi udziŵa cimene anawapatsa? Unali utawaleza.

Nthawi zambili, utawaleza umaonekela kumwamba dzuŵa likaŵala, mvula ikaleka kugwa. Utawaleza uli ndi makhala kapena kuti mitundu yambili yokongola. Kodi unauonapo utawaleza? Kodi wauona pa cithunzi-thunzi apa?

Mulungu anakamba kuti: ‘Nilonjeza kuti sinidzabweletsanso cigumula coononga anthu ndi nyama. Ndiika utawaleza mu mitambo, ndipo ukaonekela, ndizikumbukila lonjezo langa limeneli.’

Conco, kodi ukaona utawaleza, uyenela kukukumbutsa ciani? Uyenela kukukumbutsa lonjezo la Mulungu lakuti sadzaononganso dziko ndi Cigumula camadzi.

Genesis 8:18-22; 9:9-17.

Mafunso Ophunzilila

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani