LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • ll gao 5 masa. 12-13
  • Cigumula ca Nowa—Ndani Anamvetsela? Ndani Sanamvetsele?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Cigumula ca Nowa—Ndani Anamvetsela? Ndani Sanamvetsele?
  • Mvetselani kwa Mulungu Kuti Mukhale ndi Moyo Wamuyaya
  • Nkhani Zofanana
  • Cingalawa ca Nowa
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Gao 5
    Mvetselani kwa Mulungu
  • Nowa Apanga Cingalawa
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Anam’sunga “Pomupulumutsa Pamodzi ndi Anthu Ena 7”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
Onaninso Zina
Mvetselani kwa Mulungu Kuti Mukhale ndi Moyo Wamuyaya
ll gao 5 masa. 12-13

GAO 5

Cigumula ca Nowa—Ndani Anamvetsela? Ndani Sanamvetsele?

Anthu ambili m’nthawi ya Nowa anali kucita zoipa. Genesis 6:5

Angelo oipa ovala matupi a anthu akwatila akazi

Adamu ndi Hava anabala ana, ndipo anthu anaculuka padziko lapansi. M’kupita kwa nthawi, angelo ena anapanduka ndi kugwilizana ndi Satana.

Iwo anabwela padziko lapansi ndi kuvala matupi a anthu kuti akwatile akazi. Akazi amenewa anabala viŵana vikulu-vikulu vimene vinali vamphamvu ndi voopsa.

Mzimayi wanyamula mwana kwinaku ka mnyamata kamumenya; Anefili, ana a angelo oipa, acita zaciwawa

Dziko linadzala ndi anthu amene anali kucita zoipa. Baibo imakamba kuti: ‘Kuipa kwa anthu kunaculuka padziko lapansi, ndipo malingalilo onse a m’mitima ya anthu anali oipa okha-okha nthawi zonse.’

Nowa anamvetsela kwa Mulungu ndi kumanga cingalawa. Genesis 6:13, 14, 18, 19, 22

Nowa akumvetsela kwa Mulungu

Nowa anali munthu wabwino. Yehova anauza Nowa kuti adzaononga anthu oipa ndi cigumula cacikulu.

Nowa na banja lake amanga cingalawa

Mulungu anauza Nowa kumanga ciboti cacikulu cochedwa cingalawa, ndi kuloŵetsamo banja lake ndi nyama zosiyana-siyana.

Nowa acenjeza anthu za cigumula cimene cikubwela, koma akumuseka

Nowa anacenjeza anthu za Cigumula cimene cinali kubwela, koma iwo sanamvele. Ena anam’seka; ena anam’zonda.

Nowa na banja lake akusa zinyama kuti zikaloŵe m’cingalawa

Pamene Nowa anatsiliza kumanga cingalawa, analoŵetsamo nyama.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani