LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lv nkhani 3
  • Kalata Yocokela ku Bungwe Lolamulila

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kalata Yocokela ku Bungwe Lolamulila
  • “Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
  • Nkhani Zofanana
  • Kalata Yocokela ku Bungwe Lolamulila
    Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
  • ‘Yendanibe M’coonadi’
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
  • Kodi Coonadi Cikali Cofunika Masiku Ano?
    Nkhani Zina
  • Izi Ndi Zimene “Kukonda Mulungu Kumatanthauza”
    “Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
Onaninso Zina
“Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
lv nkhani 3

Kalata Yocokela ku Bungwe Lolamulila

Wokondedwa Bwenzi la Yehova:

Yesu anati: “Mudzadziŵa coonadi, ndipo coonadi cidzakumasulani.” (Yohane 8:32) Mau amenewa ndi olimbikitsa kwambili. Inde, n’zotheka ‘m’masiku otsiliza’ ano ovuta, kudziŵa coonadi ngakhale kuti mabodza afala. (2 Timoteyo 3:1) Kodi mukumbukila mmene munamvelela pamene munazindikila coonadi ca Mau a Mulungu? Mwacionekele munasangalala kwambili!

Kukhala ndi cidziŵitso colongosoka ca coonadi ndi kulalikila coonadi cimeneco mokhazikika n’kofunika. Komabe, tifunikanso kukhala ndi moyo mogwilizana ndi coonadi. Kuti ticite zimenezo, tiyenela kukhalabe m’cikondi ca Mulungu. Kodi zimenezi zimaphatikizapo kucita ciani? Mau amene Yesu anakamba pa usiku wake womaliza asanaphedwe amayankha funso limeneli. Iye anauza atumwi ake okhulupilika kuti: “Mukasunga malamulo anga, mudzakhalabe m’cikondi canga, monga mmene ine ndasungila malamulo a Atate ndi kukhalabe m’cikondi cake.”—Yohane 15:10.

Apa taona kuti Yesu anakhalabe m’cikondi ca Mulungu cifukwa anasunga malamulo a Atate wake. Ifenso tiyenela kucita cimodzimodzi masiku ano. Kuti tikhalebe m’cikondi ca Mulungu, tifunika kutsatila coonadi paumoyo wathu tsiku ndi tsiku. Pa usiku wake womaliza, Yesu anakambanso kuti: “Ngati zimenezi mukuzidziŵa, ndinu odala mukamazicita.”—Yohane 13:17.

Sitikaikila kuti buku lino lidzakuthandizani kupitiliza kutsatila coonadi paumoyo wanu, kuti mukhalebe ‘m’cikondi ca Mulungu . . . ndi kuti mukalandile moyo wosatha.’—Yuda 21.

Bungwe Lolamulila la Mboni za Yehova

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani