LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lvs tsa. 3
  • Kalata Yocokela ku Bungwe Lolamulila

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kalata Yocokela ku Bungwe Lolamulila
  • Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
  • Ŵelengani mu “m’Cikondi ca Mulungu”
  • Nkhani Zofanana
  • Cikondi Ca Mulungu N’camuyaya
    Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
  • Khalanibe M’cikondi ca Mulungu
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Musalole Kuti Cikondi Canu Cizilale
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2017
  • Izi Ndi Zimene “Kukonda Mulungu Kumatanthauza”
    “Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
Onaninso Zina
Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
lvs tsa. 3

Kalata Yocokela ku Bungwe Lolamulila

Kwa imwe okonda Yehova Mulungu na Mawu ake, Baibo:

Yesu anati: “Mudzadziŵa coonadi, ndipo coonadi cidzakumasulani.” (Yohane 8:32) Tangoganizani mmene munamvelela pamene munapeza coonadi ca m’Baibo! Cinali cinthu cokondweletsa ngako, kuona kuti m’dziko lino lodzala na mabodza, munthu n’kupeza coonadi.—2 Timoteyo 3:1.

Yehova Mulungu amafuna kuti tidziŵe coonadi. Ndipo cifukwa timakonda anthu, timafuna kuŵauzako za coonadi cimeneco. Koma kutumikila Mulungu kumaloŵetsamo zambili. Tiyenela kuyesetsa kukhala monga Akhristu, cifukwa timalemekeza kwambili mfundo za Yehova. Yesu anafotokoza njila yofunika kwambili yoonetsela kuti timakonda Mulungu. Iye anati: “Mukasunga malamulo anga, mudzakhalabe m’cikondi canga, monga mmene ine ndasungila malamulo a Atate ndi kukhalabe m’cikondi [cawo].”—Yohane 15:10.

Yesu amaŵakonda kwambili Atate wake, ndipo amacita ciliconse cimene amamuuza. Ngati tingatengele citsanzo ca Yesu mu umoyo wathu, Yehova adzatikonda kwambili, ndipo tidzapeza cimwemwe ceni-ceni. N’cifukwa cake Yesu anakamba kuti: “Ngati zimenezi mukuzidziŵa, ndinu odala mukamazicita.”—Yohane 13:17.

Tikhulupilila kuti buku ino, idzakuthandizani kudziŵa mokhalila na umoyo wogwilizana na coonadi ca m’Baibo, kuti mukhale bwenzi la Mulungu. Pemphelo lathu n’lakuti cikondi canu pa Mulungu cikule, ndipo mukhalebe “mu cikondi ca Mulungu . . . kuti mukapeze moyo wosatha.”—Yuda 21, NW.

Bungwe Lolamulila la Mboni za Yehova

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani