LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • sn nyimbo 22
  • “Yehova Ndi M’busa Wanga”

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • “Yehova Ndi M’busa Wanga”
  • Imbirani Yehova
  • Nkhani Zofanana
  • ‘Yehova ni M’busa Wanga’
    ‘Imbani Mokweza ndi Mosangalala’ kwa Yehova
  • Phunzilo 3
    Zimene Ndimaphunzila m’Baibo
  • ‘Ine Nilipo, N’tumizeni!
    ‘Imbani Mokweza ndi Mosangalala’ kwa Yehova
  • “Ine Ndilipo! Nditumizeni”
    Imbirani Yehova
Onaninso Zina
Imbirani Yehova
sn nyimbo 22

Nyimbo 22

“Yehova Ndi M’busa Wanga”

(Salmo 23)

1. Yehova ndi M’busa wanga;

Kodi ndingaopenji?

Amasamala nkhosa zake,

Sadzaziiwaladi.

Andipititsa kumadzi

Kukanditsitsimula.

Anditsogolera poyenda

M’njira zachilungamo.

Anditsogolera poyenda

M’njira zachilungamo.

2. Poyenda mumdima ndekha,

Sindidzaopa kanthu.

M’busa wanga alitu nane

Kumandilimbikitsa.

Adzozatu mutu wanga,

Wadzaza chikho changa.

Chifundo chake chinditsate,

Ndikhale m’nyumba yake.

Chifundo chake chinditsate,

Ndikhale m’nyumba yake.

3. N’ngwachikonditu M’busayo!

Ndim’tamanda mokondwa.

Ndidzalalikira kwa ena

Za chikondi chakecho.

Ndidzamvera Mawu ake

Poyenda m’njira zake.

Mwayi wanga wom’tumikira

Ndiugwiritsa ntchito.

Mwayi wanga wom’tumikira

Ndiugwiritsa ntchito.

(Onaninso Sal. 28:9; 80:1.)

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani