LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lfb phunzilo 89 tsa. 208-tsa. 209 pala. 1
  • Petulo Akana Yesu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Petulo Akana Yesu
  • Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Yesu Aphedwa
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
lfb phunzilo 89 tsa. 208-tsa. 209 pala. 1
Ku nyumba kwa Kayafa, Petulo akana Yesu kuti sam’dziŵa

PHUNZILO 89

Petulo Akana Yesu

Pamene Yesu anali na atumwi ake m’cipinda capamwamba, anaŵauza kuti: ‘Usiku uno, nonsenu mudzathaŵa na kunisiya nekha.’ Koma Petulo anati: ‘Koma osati ine! Ngakhale aŵa onse akusiyeni, ine sinidzakusiyani.’ Yesu anauza Petulo kuti: ‘Tambala akalibe kulila, iwe udzanikana katatu kuti sunidziŵa.’

Pamene asilikali anatengela Yesu ku nyumba ya Kayafa, atumwi ambili anathaŵa. Koma aŵili analondola m’cigulu ca anthu. Mmodzi wa iwo anali Petulo. Iye analoŵa mpaka m’bwalo la nyumba ya Kayafa, na kuyamba kuwotha moto. Moto utawala, mtsikana wanchito anam’zindikila Petulo, ndipo anati: ‘Nakudziŵani! Munali pamodzi na Yesu!’

Petulo anati: ‘Iyai, sindine! Nkhani imene ukamba siniidziŵa ine!’ Basi ananyamuka kuti akatuluke pa geti. Koma mtsikana winanso wanchito anamuona, ndipo anauza gulu la anthu kuti: ‘Nayenso uyu anali na Yesu!’ Koma Petulo anati: ‘Yesu uyo ine sinim’dziŵa olo pang’ono!’ Ndiyeno mwamuna wina anati: ‘Ndiwe mmodzi wa iwo! Ngakhale kakambidwe kako n’ka ku Galileya, kumene Yesu acokela.’ Koma Petulo anacita kulumbila, amvekele: ‘Ine munthu ameneyo sinim’dziŵa!’

Pa nthawi imeneyo tambala analila. Kenako Petulo anaona Yesu akuceuka kumuyang’ana. Anakumbukila mawu a Yesu, ndipo anacoka panja na kuyamba kulila kwambili.

Oweluza a Khoti Yaikulu ya Ayuda, anasonkhana ku nyumba kwa Kayafa kuti aweluze mlandu wa Yesu. Iwo anali atagwilizana kale zakuti aphe Yesu. Apa anali kungofuna kum’peza cifukwa. Koma sanam’peze na mlandu uliwonse. Kayafa anangom’funsa mwacindunji kuti: ‘Kodi ndiwe Mwana wa Mulungu?’ Yesu anayankha kuti: ‘Inde.’ Kayafa anati: ‘Basi, sipafunikilanso umboni wina. Munthu uyu akunyoza Mulungu!’ Iwo anagwilizana kuti: ‘Munthu uyu afunika kuphedwa.’ Ena anayamba kum’menya mambama, kum’thila mata, kum’phimba kumaso, kum’menya kenako n’kumuuza kuti: ‘Ngati ndiwe mneneli, tiuze wakumenya n’ndani?’

Kutaca, anatenga Yesu kupita naye ku Khoti Yaikulu ya Ayuda. Kumeneko anam’funsanso kuti: ‘Kodi ndiwe Mwana wa Mulungu?’ Yesu poyankha anati: ‘Mwakamba mwekha kuti ndine Mwana wa Mulungu.’ Basi pamenepo anam’patsa mlandu wakuti wanyoza Mulungu. Anapita naye kwa bwanamkubwa waciroma, Pontiyo Pilato. Ndiyeno cinacitika n’ciani? Tidzaona m’nkhani yokonkhapo.

“Nthawi . . . yafika kale. Mubalalika aliyense kupita kunyumba kwake, ndipo mundisiya ndekha. Koma sindikhala ndekha, cifukwa Atate ali ndi ine.”—Yohane 16:32

Mafunso: Kodi cinacitika n’ciani ku nyumba kwa Kayafa?

Kodi khoti inam’patsa mlandu wanji Yesu pomuweluza kuti aphedwe?

Mateyu 26:31-35, 57–27:2; Maliko 14:27-31, 53–15:1; Luka 22:55-71; Yohane 13:36-38; 18:15-18, 25-28

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani