Zamkati
December 1, 2013
Kodi Mulungu Ndi Wofunika kwa Ife?
© 2013 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania. All rights reserved.
NKHANI ZOPHUNZILA
FEBRUARY 3-9, 2014 | TSAMBA 8 • NYIMBO: 65, 59
“Musafulumile Kugwedezeka pa Maganizo Anu”
Tiyenela kusamala kwambili kuti tisavomeleze mfundo zokaikitsa kapena zinthu zina zimene Baibo sinafotokoze. M’buku loyamba ndi laciŵili la Atesalonika muli macenjezo a panthawi yake kwa ife tonse.
FEBRUARY 10-16, 2014 | TSAMBA 13 • NYIMBO: 40, 75
Kodi Mudzapeleka Nsembe Kaamba ka Ufumu?
Kudzimana zinthu zina n’kofunika kwambili kuti tipititse patsogolo zinthu za Ufumu. M’nkhani ino tidzaphunzila zambili pa nsembe zimene Aisiraeli anali kupeleka. Tidzaphunzilanso za anthu ambili amene amadzimana zinthu zina kaamba ka Ufumu masiku ano.
FEBRUARY 17-23, 2014 | TSAMBA 18 • NYIMBO: 109, 18
‘Ici Cidzakhala Cikumbutso kwa Inu’
FEBRUARY 24, 2014–MARCH 2, 2014 | TSAMBA 23 • NYIMBO: 99, 8
‘Citani Zimenezi Pondikumbukila’
Nthawi imene Ayuda amacita mwambo wa Pasika ndi yofananako ndi imene Akristu amacita Cikumbutso ca imfa ya Yesu. N’cifukwa ciani tiyenela kudziŵa zimene zinali kucitika pa mwambo wa Pasika? Kodi timadziŵa bwanji tsiku limene tiyenela kucita Mgonelo wa Ambuye, ndipo mwambo umenewo uli ndi phindu lanji kwa ife?
NKHANI ZINA M’MAGAZINI INO
N’kufunsilanji funso limeneli? 3
Cifukwa Cake Mulungu Ndi Wofunika kwa Ife 4
Phunzitsani Ana Anu—Yesu Kristu—Kodi Tifunika Kumukumbukila Monga Khanda Kapena Mfumu? 28
Yandikilani kwa Mulungu—“Taonani! Zinthu Zonse Zimene Ndikupanga N’zatsopano” 30
Mlozela nkhani wa magazini a Nsanja ya Mlonda a 2013 31