LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w14 1/1 tsa. 3
  • Mphamvu ya Imfa

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mphamvu ya Imfa
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Munthu Akamwalila, Cimacitikano N’ciyani?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • ‘Apanga Zinthu Zonse Kukhala Zatsopano’
    ‘Imbani Mokweza ndi Mosangalala’ kwa Yehova
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
w14 1/1 tsa. 3

NKHANI YA PACIKUTO | KODI IMFA NDI MAPETO A ZONSE?

Mphamvu ya Imfa

Imfa si nkhani yosangalatsa. Ndipo anthu ambili samakonda kukambitsilana za imfa. Koma imfa sithawika. Iyo ndi yamphamvu ndipo ululu wake ndi waukulu kwambili.

Palibe cimene tingacite kuti tikonzekele imfa ya makolo, mkazi, mwamuna kapena ya mwana wathu. Mavuto ena angacitike mwadzidzidzi, koma ena angatenge nthawi yaitali. Mulimonse mmene zingakhalile, ululu wa imfa sitingaupewe, ndipo zotsatilapo zake zimakhala zophweteka kwambili.

Antonio, amene atate wake anamwalila pangozi ya galimoto, anati: “Zimakhala ngati winawake wakhoma zitseko zonse za nyumba yanu ndi kutenga makiyi ndipo sungakwanitse kuloŵa m’nyumba. Zinthu zikafika apa umasoŵa cocita. Sungatsimikize kuti zimenezo zacitikadi cifukwa ndi zinthu zopanda cilungamo. Koma popeza zinthu zacitika kale, palibe cimene ungacite.”

A Dorothy naonso amene anataikilidwa wokondedwa wao, ndipo anakhala wamasiye ali ndi zaka 47, anafuna kupeza mayankho pa mafunso okhudza imfa. Pokhala m’phunzitsi wa ana m’cipembedzo cao, io anali kukhulupilila kuti imfa si mapeto a zonse. Komabe, sanali kudziŵa bwino zimene zimacitika munthu akamwalila. Tsiku lina, anafunsa bambo wa chalichi ca Anglican kuti: “Kodi cimacitika n’ciani munthu akamwalila?” Bamboyo anati: “Palibe amene adziŵa zimene zimacitika, tingofunika kuyembekezela.”

Kodi tifunika kukhalabe conco n’kumangoyembekezela? Kodi pali njila ina iliyonse imene tingadziŵile kaya imfa ndi mapeto a zonse?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani