LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w14 3/1 tsa. 6
  • Cocitika Cimene Simuyenela Kuphonya

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Cocitika Cimene Simuyenela Kuphonya
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Nkhani Zofanana
  • Kukumbukila Imfa ya Yesu—Liti Ndipo Kuti?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • ‘Citani Zimenezi Pondikumbukila’
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Zimene Mwambo Wosalila Zambili Umatiphunzitsa Ponena za Mfumu Yathu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2019
  • Cifukwa Cake Timacita Mgonelo wa Ambuye
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
w14 3/1 tsa. 6

NKHANI YA PACIKUTO | ZIMENE MULUNGU WAKUCITILANI

Cocitika Cimene Simuyenela Kuphonya

Usiku wakuti maŵa apeleka moyo wake, Yesu anauza otsatila ake okhulupilika kuti azikumbukila imfa yake. Pogwilitsila nchito mkate wopanda cotupitsa ndi vinyo wofiila, iye anayambitsa cimene cimachedwa kuti Cakudya ca Madzulo kapena kuti Mgonelo wa Ambuye ndipo anawauza kuti: “Muzicita zimenezi pondikumbukila.”—Luka 22:19.

Caka ciliconse, Mboni za Yehova padziko lonse zimasonkhana kuti zikumbukile imfa ya Yesu. Cikumbutso ca mu 2014 cidzacitika pa Mande, April 14 dzuŵa litaloŵa.

Tikuitanani kuti mukapezeke pamsonkhano umenewu. Padzakambidwa nkhani imene idzafotokoza cifukwa cake imfa ya Yesu ndi yofunika. Simufunikila kupeleka ndalama kuti mukapezeke pa cocitika cimeneci. Ndiponso sipadzakhala kusonkhetsa ndalama. Munthu amene wakupatsani magazini ino adzakuuzani nthawi ndi malo kumene kudzacitikila Cikumbutso m’dela lanu, kapena mungafufuze pa Webusaiti yathu ya jw.org. Conde lembani penapake zimenezi kuti musakaphonye cocitika cimeneci.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani